1Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya;
2Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya,
3Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga,
4‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya.
5Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova,
6Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova?
7Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri;
8Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu?
9Mumalamula nyanja ya mafunde awukali;
10Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa;
11Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu;
12Munalenga Kumpoto ndi Kummwera;
13Mkono wanu ndi wamphamvu;
14Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu;
15Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu,
16Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu;
17Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo
18Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova,
19Kale munayankhula mʼmasomphenya,
20Ndamupeza mtumiki wanga Davide;
21Dzanja langa lidzamuchirikiza;
22Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho;
23Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake
24Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye,
25Ndidzayika dzanja lake pa nyanja,
26Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga,
27Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa;
28Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya,
29Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya,
30“Ngati ana ake adzataya lamulo langa
31ngati adzaswa malamulo anga
32Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo,
33Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye,
34Sindidzaswa pangano langa
35Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga
36kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya
37udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi,
38“Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya,
39Mwakana pangano ndi mtumiki wanu
40Inu mwagumula makoma ake onse
41Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake;
42Mwakweza dzanja lamanja la adani ake;
43Mwabunthitsa lupanga lake,
44Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake
45Mwachepetsa masiku a unyamata wake;
46“Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale?
47Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa
48Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa?
49Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija,
50Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera,
51mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova,
52“Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!”