1Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa,
2Pemphero langa lifike pamaso panu;
3Pakuti ndili ndi mavuto ambiri
4Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje;
5Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa,
6Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni,
7Ukali wanu ukundipsinja kwambiri,
8Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni
9maso anga ada ndi chisoni.
10Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa?
11Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda,
12Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima,
13Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo;
14Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana
15Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa;
16Ukali wanu wandimiza;
17Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula;
18Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga;