1Yehova munakomera mtima dziko lanu;
2Munakhululukira mphulupulu za anthu anu
3Munayika pambali ukali wanu wonse
4Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,
5Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?
6Kodi simudzatitsitsimutsanso,
7Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova,
8Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena;
9Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye,
10Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi;
11Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi,
12Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino,
13Wolungama amapita patsogolo pake