1Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa;
2Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo,
3zimene tinazimva ndi kuzidziwa,
4Sitidzabisira ana awo,
5Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo
6kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa,
7Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu
8Iwo asadzakhale monga makolo awo,
9Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta,
10iwo sanasunge pangano la Mulungu
11Anayiwala zimene Iye anachita,
12Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona,
13Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo,
14Anawatsogolera ndi mtambo masana
15Iye anangʼamba miyala mʼchipululu
16Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala
17Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye,
18Ananyoza Mulungu mwadala
19Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti,
20Iye atamenya thanthwe
21Yehova atawamva anakwiya kwambiri;
22pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu
23Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba
24anagwetsa mana kuti anthu adye,
25Anthu anadya buledi wa angelo,
26Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba,
27Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi,
28Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo,
29Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka
30Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho,
31mkwiyo wa Mulungu unawayakira;
32Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa;
33Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya.
34Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo;
35Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo,
36Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo,
37Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye,
38Komabe Iye anali wachifundo;
39Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe,
40Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu
41Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu;
42Sanakumbukire mphamvu zake,
43tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto,
44Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi;
45Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga,
46Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala,
47Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala
48Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala,
49Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo,
50Analolera kukwiya,
51Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto,
52Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto;
53Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha
54Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera,
55Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo
56Koma iwo anayesa Mulungu
57Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo,
58Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano;
59Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri;
60Anasiya nyumba ya ku Silo,
61Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo,
62Anapereka anthu ake ku lupanga;
63Moto unanyeketsa anyamata awo,
64ansembe awo anaphedwa ndi lupanga,
65Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo,
66Iye anathamangitsa adani ake;
67Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe,
68Koma anasankha fuko la Yuda,
69Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda,
70Anasankha Davide mtumiki wake
71kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa
72Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama;