1Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo;
2Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye;
3Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula;
4Munagwira zikope zanga kuti ndisagone
5Ndinaganizira za masiku akale,
6Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku.
7“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya?
8Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu?
9Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima?
10Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso:
11Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova;
12Ndidzakumbukira ntchito zanu
13Njira zanu Mulungu ndi zoyera.
14Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa;
15Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu,
16Madzi anakuonani Mulungu,
17Mitambo inakhuthula madzi ake pansi,
18Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu,
19Njira yanu inadutsa pa nyanja,
20Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa