1Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli,
2Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka;
3Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira,
4Iwo alibe zosautsa;
5Saona mavuto monga anthu ena;
6Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo;
7Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa;
8Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa;
9Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba
10Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo
11Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji?
12Umu ndi mmene oyipa alili;
13Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera;
14Tsiku lonse ndapeza mavuto;
15Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,”
16Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi,
17kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu;
18Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera;
19Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa,
20Monga loto pamene wina adzuka,
21Pamene mtima wanga unasautsidwa
22ndinali wopusa ndi wosadziwa;
23Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse;
24Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu
25Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu?
26Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka,
27Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka;
28Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu.