1Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo,
2Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo,
3Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu,
4Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu
5Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse,
6Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa
7Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika;
8Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina
9Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake
10Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali
11Mafumu onse adzamuweramira
12Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira,
13Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa
14Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa
15Iye akhale ndi moyo wautali;
16Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse;
17Dzina lake likhazikike kwamuyaya,
18Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli
19Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya
20Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.