1Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo;
2Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu,
3Mukhale thanthwe langa lothawirapo,
4Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa,
5Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse,
6Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu;
7Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri
8Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu,
9Musanditaye pamene ndakalamba;
10Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane;
11Iwo amati, “Mulungu wamusiya;
12Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu,
13Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi,
14Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse,
15Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu,
16Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse.
17Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa,
18Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu
19Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba.
20Ngakhale mwandionetsa mavuto
21Inu mudzachulukitsa ulemu wanga
22Ndidzakutamandani ndi zeze
23Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe
24Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo