1Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2Imbani ulemerero wa dzina lake;
3Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu!
4Dziko lonse lapansi limaweramira inu;
5Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita,
6Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma,
7Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya,
8Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu,
9Iye watchinjiriza miyoyo yathu
10Pakuti Inu Mulungu munatiyesa;
11Inu mwatilowetsa mʼndende
12Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu;
13Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza
14Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza
15Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu
16Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu.
17Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga,
18Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga
19koma ndithu Mulungu wamvetsera
20Matamando akhale kwa Mulungu