1Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha;
2Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;
3Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti?
4Iwo akufunitsitsa kumugwetsa
5Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga;
6Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;
7Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu:
8Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu;
9Anthu wamba ndi mpweya chabe;
10Musadalire kulanda mwachinyengo
11Mulungu wayankhula kamodzi,
12komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika.