1Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma
2Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse
3Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu;
4Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso
5Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu,
6Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi;
7Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;
8Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya;
9Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka;
10Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu;
11Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako;
12Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso,
13Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake,
14Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu;
15Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo;
16Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako;
17Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse;