1Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu;
2Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena
3Sanalande dziko ndi lupanga lawo,
4Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga
5Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu;
6Sindidalira uta wanga,
7koma Inu mumatigonjetsera adani athu,
8Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse,
9Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa;
10Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani
11Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa
12Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika,
13Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina,
14Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina;
15Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse
16chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe,
17Zonsezi zinatichitikira
18Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo;
19Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe
20Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu
21kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi,
22Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse,
23Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona!
24Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu,
25Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi;
26Imirirani ndi kutithandiza,