1Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane;
2Tengani chishango ndi lihawo;
3Tengani mkondo ndi nthungo,
4Iwo amene akufunafuna moyo wanga
5Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo
6Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera
7Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa
8chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa
9Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova
10Thupi langa lidzafuwula mokondwera,
11Mboni zopanda chisoni zinayimirira,
12Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino
13Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli
14ndinayendayenda ndi kulira maliro,
15Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala;
16Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe;
17Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana?
18Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu;
19Musalole adani anga onyenga
20Iwowo sayankhula mwamtendere,
21Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa!
22Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete.
23Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza!
24Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga.
25Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!”
26Onse amene amakondwera ndi masautso anga
27Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa,
28Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu