1Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama,
2Mutamandeni Yehova ndi pangwe;
3Muyimbireni nyimbo yatsopano;
4Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona;
5Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama;
6Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa,
7Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko;
8Dziko lonse lapansi liope Yehova;
9Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo;
10Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina;
11Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya,
12Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova,
13Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi
14kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira
15Iye amene amapanga mitima ya onse,
16Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo;
17Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso,
18Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye;
19kuwawombola iwo ku imfa
20Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo;
21Mwa Iye mitima yathu imakondwera,
22Chikondi chanu chosatha