1Inu Yehova, mfumu ikusangalala mu mphamvu yanu,
2Inu mwayipatsa zokhumba za mtima wake
3Inu munayilandira ndi madalitso ochuluka
4Iye anakupemphani moyo, ndipo munamupatsa
5Kudzera mʼzigonjetso zimene munapereka, ulemerero wake ndi waukulu;
6Zoonadi Inu mwayipatsa madalitso amuyaya,
7Pakuti mfumu imadalira Yehova;
8Dzanja lanu lidzayimitsa adani anu onse;
9Pa nthawi ya kuonekera kwanu
10Inu mudzawononga ana awo pa dziko lapansi,
11Ngakhale iwo akukonzereni chiwembu mwa kuchenjera kwawo
12pakuti mudzawapirikitsa ndipo adzaonetsa misana yawo
13Mukwezeke Inu Yehova mʼmphamvu yanu,