We Believe JesusFé, Esperança e Nova Vida

Masalimo 18

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero · nianja

← Masalimo 17 Masalimo Masalimo 19 →

1Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.

2Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga;

3Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando,

4Zingwe za imfa zinandizinga;

5Anandimanga ndi zingwe za ku manda;

6Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova;

7Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi,

8Mʼmphuno mwake munatuluka utsi;

9Iye anangʼamba thambo natsika pansi;

10Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka;

11Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake,

12Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala,

13Yehova anabangula kumwamba ngati bingu,

14Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake,

15Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera;

16Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira;

17Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,

18Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto,

19Iye anandipititsa kumalo otakasuka;

20Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa;

21Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova;

22Malamulo ake onse ali pamaso panga;

23Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake

24Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa,

25Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu;

26kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu,

27Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa,

28Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe;

29Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo;

30Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro;

31Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova?

32Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu

33Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi;

34Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

35Inu mumandipatsa chishango chachipambano,

36Munakulitsa njira yoyendamo ine,

37Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira;

38Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka;

39Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo,

40Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa,

41Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa.

42Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo.

43Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu;

44Alendo amadzipereka okha pamaso panga;

45Iwo onse anataya mtima;

46Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa!

47Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango,

48amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga.

49Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova;

50Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake;

← Masalimo 17 Masalimo Masalimo 19 →