1Landitseni Yehova kwa anthu oyipa;
2amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa
3Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka;
4Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa;
5Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika;
6Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
7Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu,
8Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova;
9Mitu ya amene andizungulira
10Makala amoto agwere pa iwo;
11Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko;
12Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka,
13Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu,