1Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino.
2Yamikani Mulungu wa milungu.
3Yamikani Ambuye wa ambuye,
4Iye yekhayo amene amachita zodabwitsa zazikulu,
5Amene mwachidziwitso chake anapanga mayiko akumwamba,
6Amene anayala dziko lapansi pamwamba pa madzi,
7Amene anapanga miyuni ikuluikulu,
8Dzuwa lilamulire usana,
9Mwezi ndi nyenyezi zilamulire usiku,
10Amene anakantha ana woyamba kubadwa a Igupto,
11Natulutsa Israeli pakati pawo,
12Ndi dzanja lamphamvu ndi mkono wotambasuka,
13Amene anagawa Nyanja Yofiira pakati,
14Nadutsitsa Israeli pakati pa nyanjayo,
15Koma anakokolola Farao ndi ankhondo ake mʼNyanja Yofiira,
16Amene anatsogolera anthu ake mʼchipululu
17Amene anakantha mafumu akuluakulu,
18Napha mafumu amphamvu,
19Siloni mfumu ya Aamori,
20Ogi mfumu ya Basani,
21Napereka dziko lawo ngati cholowa,
22Cholowa cha mtumiki wake Israeli;
23Amene anatikumbukira ife anthu opeputsidwa,
24Amene anatimasula kwa adani athu,
25Amene amapereka chakudya kwa cholengedwa chilichonse,
26Yamikani Mulungu wakumwamba,