1Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa,
2Odala ndi amene amasunga malamulo ake,
3Sachita cholakwa chilichonse;
4Inu mwapereka malangizo
5Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika
6Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi,
7Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama,
8Ndidzamvera zophunzitsa zanu;
9Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake?
10Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse;
11Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga
12Mutamandike Inu Yehova;
13Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse
14Ndimakondwera potsatira malamulo anu
15Ndimalingalira malangizo anu
16Ndimakondwera ndi malamulo anu;
17Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;
18Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona
19Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;
20Moyo wanga wafowoka polakalaka
21Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa,
22Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo
23Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza,
24Malamulo anu amandikondweretsa;
25Moyo wanga wakangamira fumbi;
26Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha;
27Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu;
28Moyo wanga wafowoka ndi chisoni;
29Mundichotse mʼnjira zachinyengo;
30Ndasankha njira ya choonadi;
31Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova;
32Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu,
33Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu;
34Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu
35Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu,
36Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu,
37Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe;
38Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu,
39Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa,
40Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu!
41Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova,
42ndipo ndidzayankha amene amandinyoza,
43Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga,
44Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse,
45Ndidzayendayenda mwaufulu,
46Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu
47popeza ndimakondwera ndi malamulo anu
48Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda,
49Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu,
50Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi:
51Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa,
52Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale,
53Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa
54Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga
55Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova,
56Ichi ndicho ndakhala ndikuchita:
57Yehova, Inu ndiye gawo langa;
58Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse;
59Ndinalingalira za njira zanga
60Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza
61Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe,
62Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu
63Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani,
64Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika,
65Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu
66Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino,
67Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera,
68Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino;
69Ngakhale odzikuza andipaka mabodza,
70Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa,
71Ndi bwino kuti ndinasautsidwa
72Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri
73Manja anu anandilenga ndi kundiwumba;
74Iwo amene amakuopani akondwere akandiona,
75Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama
76Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa,
77Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo,
78Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa;
79Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine,
80Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu
81Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu,
82Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu;
83Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi
84Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti?
85Anthu osalabadira za Mulungu,
86Malamulo anu onse ndi odalirika;
87Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi
88Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,
89Mawu anu Yehova ndi amuyaya;
90Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse;
91Malamulo anu alipobe mpaka lero lino,
92Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa,
93Ine sindidzayiwala konse malangizo anu,
94Ndine wanu, ndipulumutseni;
95Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge,
96Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire,
97Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu!
98Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga,
99Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse
100Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba,
101Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa
102Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu,
103Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa,
104Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu;
105Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga
106Ndalumbira ndipo ndatsimikiza,
107Ndazunzika kwambiri;
108Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga,
109Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi,
110Anthu oyipa anditchera msampha,
111Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya;
112Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu
113Ndimadana ndi anthu apawiripawiri,
114Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa;
115Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa,
116Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;
117Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa;
118Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu,
119Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala;
120Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu;
121Ndachita zolungama ndi zabwino;
122Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino,
123Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu,
124Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,
125Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa,
126Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu;
127Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu
128ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka,
129Maumboni anu ndi odabwitsa
130Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika;
131Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu,
132Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo,
133Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu;
134Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza,
135Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu
136Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga,
137Yehova ndinu wolungama,
138Maumboni amene munatipatsa ndi olungama;
139Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga
140Mawu anu ndi woyera kwambiri
141Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka,
142Chilungamo chanu nʼchamuyaya,
143Mavuto ndi masautso zandigwera,
144Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse;
145Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova,
146Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni
147Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo;
148Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku,
149Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;
150Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira,
151Koma Inu Yehova muli pafupi,
152Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu
153Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse,
154Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola;
155Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa,
156Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu;
157Adani amene akundizunza ndi ambiri,
158Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro,
159Onani momwe ndimakondera malangizo anu;
160Mawu anu onse ndi owona;
161Olamulira amandizunza popanda chifukwa,
162Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu,
163Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho,
164Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku
165Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu,
166Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova,
167Ndimamvera umboni wanu
168Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu,
169Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova;
170Kupempha kwanga kufike pamaso panu;
171Matamando asefukire pa milomo yanga,
172Lilime langa liyimbe mawu anu,
173Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza
174Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova,
175Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni,
176Ndasochera ngati nkhosa yotayika,