1Tamandani Yehova.
2Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;
3Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,
4Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;
5Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,
6Ndithu sadzagwedezeka;
7Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;
8Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;
9Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,
10Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;