1Tamandani Yehova.
2Ntchito za Yehova nʼzazikulu;
3Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu,
4Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike;
5Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye;
6Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake,
7Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama;
8Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi,
9Iyeyo amawombola anthu ake;
10Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru;