1Mulungu amene ndimakutamandani,
2pakuti anthu oyipa ndi achinyengo
3Andizungulira ndi mawu audani,
4Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza,
5Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino,
6Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye;
7Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa,
8Masiku ake akhale owerengeka;
9Ana ake akhale amasiye
10Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha;
11Wokongoza alande zonse zimene ali nazo;
12Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima
13Zidzukulu zake zithe nʼkufa,
14Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova;
15Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse,
16Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo,
17Anakonda kutemberera,
18Anavala kutemberera ngati chovala;
19Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho,
20Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga,
21Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse,
22Pakuti ndine wosauka ndi wosowa,
23Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo,
24Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya,
25Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane;
26Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga;
27Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu,
28Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa;
29Onditsutsa adzavekedwa mnyozo,
30Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri;
31Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo,