1Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
2Owomboledwa a Yehova anene zimenezi
3iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,
4Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,
5Iwo anamva njala ndi ludzu,
6Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo
7Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka
8Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
9pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu
10Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu,
11pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu
12Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga;
13Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
14Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu
15Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
16pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa
17Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira,
18Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse
19Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
20Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa;
21Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
22Apereke nsembe yachiyamiko
23Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi;
24Anaona ntchito za Yehova,
25Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho
26Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya;
27Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera;
28Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
29Yehova analetsa namondwe,
30Anali osangalala pamene kunakhala bata,
31Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
32Akuze Iye mu msonkhano wa anthu
33Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu,
34ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere,
35Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi
36kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako,
37Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa
38Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri,
39Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa
40Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka
41Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo
42Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala,
43Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi