1Yamikani Yehova, itanani dzina lake;
2Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo;
3Munyadire dzina lake loyera;
4Dalirani Yehova ndi mphamvu zake;
5Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita,
6inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake,
7Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;
8Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya,
9pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu,
10Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa,
11“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani
12Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero,
13ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina,
14Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza;
15“Musakhudze odzozedwa anga;
16Iye anabweretsa njala pa dziko
17Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo,
18Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza,
19mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa,
20Mfumu inatuma munthu kukamumasula,
21Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake,
22kulangiza ana a mfumu monga ankafunira
23Tsono Israeli analowa mu Igupto;
24Yehova anachulukitsa anthu ake;
25amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake,
26Yehova anatuma Mose mtumiki wake,
27Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo,
28Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima.
29Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi,
30Dziko lawo linadzaza ndi achule
31Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka
32Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala,
33Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu,
34Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera,
35zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo,
36Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo,
37Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri,
38Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka,
39Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo,
40Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri
41Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka;
42Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene
43Iye anatulutsa anthu ake akukondwera,
44Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina
45kuti iwo asunge malangizo ake