1Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi,
2kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru
3Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi.
4koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu;
5Mapazi ake amatsikira ku imfa;
6Iye saganizirapo za njira ya moyo;
7Tsopano ana inu, mundimvere;
8Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo,
9kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena;
10kapenanso alendo angadyerere chuma chako
11Potsiriza pa moyo wako udzabuwula,
12Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo!
13Sindinamvere aphunzitsi anga
14Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke
15Imwa madzi a mʼchitsime chakochako,
16Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu?
17Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha,
18Yehova adalitse kasupe wako,
19Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino.
20Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo?
21Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona,
22Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha;
23Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo,