We Believe JesusFé, Esperança e Nova Vida

Miyambo 4

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero · nianja

← Miyambo 3 Miyambo Miyambo 5 →

1Ananu, mverani malangizo a abambo anu;

2Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino.

3Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga;

4Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti,

5Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu;

6Usasiye nzeru ndipo idzakusunga.

7Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru.

8Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza;

9Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako;

10Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena,

11Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru.

12Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana;

13Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi.

14Usayende mʼnjira za anthu oyipa

15Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo;

16Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa;

17Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi

18Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha

19Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani;

20Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena;

21Usayiwale malangizo angawa,

22Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza

23Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu

24Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota;

25Maso ako ayangʼane patsogolo;

26Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako

27Usapatukire kumanja kapena kumanzere;

← Miyambo 3 Miyambo Miyambo 5 →