1Ananu, mverani malangizo a abambo anu;
2Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino.
3Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga;
4Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti,
5Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu;
6Usasiye nzeru ndipo idzakusunga.
7Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru.
8Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza;
9Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako;
10Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena,
11Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru.
12Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana;
13Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi.
14Usayende mʼnjira za anthu oyipa
15Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo;
16Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa;
17Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi
18Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha
19Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani;
20Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena;
21Usayiwale malangizo angawa,
22Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza
23Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu
24Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota;
25Maso ako ayangʼane patsogolo;
26Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako
27Usapatukire kumanja kapena kumanzere;