1Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola,
2Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira,
3Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu,
4Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake,
5Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake,
6Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga
7Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu
8Kupereka ulemu kwa chitsiru
9Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa
10Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda,
11Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake
12Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo
13Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango,
14Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake,
15Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale;
16Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru
17Munthu wongolowera mikangano imene si yake
18Monga munthu wamisala amene
19ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake,
20Pakasowa nkhuni, moto umazima;
21Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto,
22Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma;
23Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi
24Munthu wachidani amayankhula zabwino
25Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire,
26Ngakhale amabisa chidani mochenjera,
27Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha;
28Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka,