1Usachitire nsanje anthu oyipa,
2pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa,
3Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru,
4Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake
5Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri,
6Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo.
7Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru;
8Amene amakonzekera kuchita zoyipa
9Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo,
10Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti
11Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe;
12Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,”
13Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino;
14Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako;
15Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa.
16paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso.
17Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako.
18Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo,
19Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa
20paja munthu woyipa alibe tsogolo.
21Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu,
22awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi.
23Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa:
24Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,”
25Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino
26Woyankhula mawu owona
27Ugwiriretu ntchito zako zonse,
28Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa,
29Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine;
30Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi
31Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga,
32Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga
33Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,”
34umphawi udzafika pa iwe ngati mbala