1Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga
2ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru
3ngati upempha kuti uzindikire zinthu
4ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva
5ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova;
6Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru,
7Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo.
8pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama.
9Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo,
10Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako,
11Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga;
12Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa,
13amene amasiya njira zolungama
14amene amakondwera pochita zoyipa
15Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota,
16Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo;
17amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake
18Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa;
19Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera
20Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino,
21Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko
22Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo,