1Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo;
3kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru,
4Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera,
5Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake,
6kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo,
7Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru.
8Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako
9Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako
10Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa
11Akadzati, “Tiye kuno;
12tiwameze amoyo ngati manda,
13Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali
14Bwera, chita nafe maere,
15Mwana wanga, usayende nawo pamodzi,
16Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha,
17Nʼkopanda phindu kutchera msampha
18Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe;
19Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza;
20Nzeru ikufuwula mu msewu,
21ikufuwula pa mphambano ya misewu,
22“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti?
23Tamverani mawu anga a chidzudzulo.
24Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera.
25Uphungu wanga munawunyoza.
26Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto;
27Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe,
28“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha;
29Popeza iwo anadana ndi chidziwitso
30popeza iwo sanasamale malangizo anga
31Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo
32Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo,
33Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata;