We Believe JesusFé, Esperança e Nova Vida

Miyambo 16

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero · nianja

← Miyambo 15 Miyambo Miyambo 17 →

1Zolinga za mu mtima ndi za munthu,

2Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake,

3Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova,

4Yehova amachita zonse ndi cholinga chake,

5Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova.

6Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake;

7Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova,

8Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo,

9Mtima wa munthu umalingalira zochita,

10Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu;

11Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova;

12Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu,

13Mawu owona amakondweretsa mfumu.

14Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa,

15Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo;

16Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide.

17Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa;

18Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko,

19Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa,

20Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino,

21A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu,

22Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako,

23Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru,

24Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi,

25Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu

26Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira;

27Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa

28Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano,

29Munthu wandewu amakopa mnansi wake,

30Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota;

31Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero;

32Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo,

33Maere amaponyedwa pa mfunga,

← Miyambo 15 Miyambo Miyambo 17 →