We Believe JesusFé, Esperança e Nova Vida

Miyambo 13

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero · nianja

← Miyambo 12 Miyambo Miyambo 14 →

1Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake,

2Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake,

3Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake,

4Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu,

5Munthu wolungama amadana ndi zabodza,

6Chilungamo chimateteza munthu wangwiro,

7Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse;

8Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake,

9Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa,

10Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano,

11Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono

12Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima,

13Amene amanyoza malangizo adzawonongeka,

14Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo;

15Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu,

16Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru,

17Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto,

18Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa,

19Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima,

20Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru;

21Choyipa chitsata mwini,

22Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa,

23Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri,

24Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda,

25Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta,

← Miyambo 12 Miyambo Miyambo 14 →