1“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso
2Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake,
3Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse
4Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka.
5Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa
6Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’
7Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake.
8Zirombo zimakabisala
9Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake,
10Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi
11Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula,
12Mulungu amayendetsa mitamboyo
13Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu,
14“Abambo Yobu, tamvani izi;
15Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo
16Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo,
17Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta
18kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo
19“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye;
20Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu?
21Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa,
22Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto;
23Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa;
24Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri,