1Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere,
3Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake,
4Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu
5Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo;
6Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga;
7“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa?
8Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu?
9Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa?
10Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu,
11Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira,
12Chifukwa chiyani ukupsa mtima,
13moti ukupsera mtima Mulungu
14“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima
15Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake,
16nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota,
17“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera;
18zimene anandiphunzitsa anthu anzeru,
19(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa
20Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake,
21Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake,
22Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa;
23Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya;
24Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri;
25chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu
26Amapita mwa mwano kukalimbana naye
27“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa
28munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka
29Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa,
30Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo;
31Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe,
32Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane,
33Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse,
34Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala
35Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa;