1Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi;
3Kodi mawu anu ochulukawo adzatha?
4Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu,
5Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani;
6“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa;
7Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu;
8Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni;
9Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane,
10Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza;
11Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa
12Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya;
13anthu ake oponya mauta andizungulira.
14Akundivulaza kawirikawiri,
15“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa
16Maso anga afiira ndi kulira,
17komatu manja anga sanachite zachiwawa
18“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga;
19Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba;
20Wondipembedzera ndi bwenzi langa,
21iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu
22“Pakuti sipapita zaka zambiri