1Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
2“Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa?
3Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku?
4Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika
5Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula
6ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake,
7“Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu?
8Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani?
9Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi
10“Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende
11Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo;
12Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru
13“Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye
14ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako
15udzatukula mutu wako wosachita manyazi;
16Udzayiwala ndithu zowawa zako,
17Moyo wako udzawala kupambana usana,
18Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo;
19Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza
20Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza,