1“Ine ndatopa nawo moyo wanga;
2Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa,
3Kodi mumakondwera mukamandizunza,
4Kodi maso anu ali ngati a munthu?
5Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu,
6kuti Inu mufufuze zolakwa zanga
7ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa
8“Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu.
9Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi,
10Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale,
11Munandikuta ndi khungu ndi mnofu
12Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu,
13“Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu,
14Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa
15Ngati ndili wolakwa, tsoka langa!
16Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango
17Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane
18“Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe?
19Ndikanapanda kubadwa,
20Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha?
21ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako
22ku dziko la mdima wandiweyani