1“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera?
2Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere?
3Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo;
4Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo;
5“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera?
6Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake,
7Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda;
8Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu
9“Kodi njati ingavomere kukutumikira?
10Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima?
11Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake?
12Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako
13“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira,
14Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi
15nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa,
16Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake;
17Chifukwa Mulungu anayimana nzeru,
18Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga,
19“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo
20Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira,
21Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake,
22Iye sachita mantha, saopa chilichonse;
23Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake
24Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha;
25Lipenga likalira amati, ‘Twee!’
26“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako,
27Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka
28Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku;
29Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye;
30Ana ake amayamwa magazi,