1Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2“Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu?
3Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama?
4“Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula,
5Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu?
6Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa;
7Sunawapatse madzi anthu otopa,
8ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake,
9Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu,
10Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira,
11nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu,
12“Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba?
13Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani?
14Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona
15Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale
16Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane,
17Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni!
18Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino,
19“Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera;
20Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka
21“Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere;
22Landira malangizo a pakamwa pake
23Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa;
24ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi,
25Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako,
26Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse
27Udzamupempha ndipo adzakumvera,
28Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi,
29Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’
30Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa,