1Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2“Mvetserani bwino mawu anga;
3Ndiloleni ndiyankhule
4“Kodi ine ndikudandaulira munthu?
5Ndipenyeni ndipo mudabwe;
6Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri;
7Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo,
8Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo,
9Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha;
10Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa;
11Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa;
12Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze;
13Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero
14Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’
15Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire?
16Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo,
17“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa?
18Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo,
19Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’
20Mulole kuti adzionere yekha chilango chake,
21Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo,
22“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru,
23Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse,
24thupi lake lili lonenepa,
25Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima,
26Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda
27“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza,
28Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti,
29Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo?
30Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka,
31Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo?
32Iye amanyamulidwa kupita ku manda
33Dothi la ku chigwa limamukomera;
34“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo