1“Munthu wobadwa mwa amayi
2Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota;
3Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa?
4Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa?
5Masiku a munthu ndi odziwikiratu;
6Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule
7“Mtengo uli nacho chiyembekezo:
8Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka
9koma pamene chinyontho chafika udzaphukira
10Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda,
11Monga madzi amaphwera mʼnyanja
12momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso;
13“Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda
14Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo?
15Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani;
16Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga
17Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba;
18“Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka
19monganso madzi oyenda amaperesera miyala
20Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu;
21Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo;
22Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake