1Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2“Ndithudi inuyo ndinu anthu
3Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu;
4“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga,
5Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka.
6Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere,
7“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa,
8kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa,
9Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa
10Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse,
11Kodi khutu sindiye limene limamva mawu
12Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba?
13“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu;
14Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso.
15Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma;
16Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana;
17Iye amalanda aphungu nzeru zawo
18Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo
19Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo
20Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika
21Iye amanyoza anthu otchuka
22Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima
23Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso;
24Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi;
25Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira;