1Anthu olungama amafa,
2Iwo amene amakhala moyo wolungama
3“Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa,
4Kodi inu mukuseka yani?
5Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu,
6Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu.
7Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali.
8Mʼnyumba mwanu mwayika
9Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta
10Inu mumatopa ndi maulendo anu,
11“Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa,
12Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama,
13Pamene mufuwula kupempha thandizo,
14Ndipo panamveka mawu akuti,
15Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse,
16Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya
17Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera;
18Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa;
19anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo.
20Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka,
21“Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.