1“Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja!
2“Ndani anadzutsa wochokera kummawa
3Amawalondola namayenda mosavutika,
4Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza,
5Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa;
6aliyense akuthandiza mnzake
7Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide,
8“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga,
9Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi,
10Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe;
11“Onse amene akupsera mtima
12Udzafunafuna adani ako,
13Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako,
14Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi,
15“Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu
16Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso
17“Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi,
18Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma,
19Mʼchipululu ndidzameretsa
20kuti anthu aone ndi kudziwa;
21“Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’
22Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze
23tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani,
24Koma inu sindinu kanthu
25“Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera,
26Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe,
27Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’
28Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe,
29Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo!