1Tsiku limenelo,
2Tsiku limenelo Yehova adzati,
3Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira;
4Ine sindinakwiye.
5Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze;
6Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu,
7Kodi Yehova anakantha Israeli
8Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo,
9Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo.
10Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja,
11Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka
12Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
13Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.