1Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya:
2Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya,
3Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi;
4Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga;
5Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione
6Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta
7Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta,
8zonse zoteteza Yuda zachotsedwa.
9inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide
10Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu
11Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime
12Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse
13Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala;
14Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
15Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti,
16Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo
17“Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba
18Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira
19Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako
20“Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
21Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
22Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
23Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
24Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
25“Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’ ” Yehova wayankhula chomwechi.