1Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo,
2kuwalanda anthu osauka ufulu wawo
3Kodi mudzatani pa tsiku la chilango,
4Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa
5“Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga,
6Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu,
7Koma izi si zimene akufuna kukachita,
8Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’
9‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi?
10Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano,
11nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake
12Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake.
13Pakuti mfumuyo ikuti,
14Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu
15Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito,
16Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse
17Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto,
18Ankhondo ake adzawonongedwa
19Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri,
20Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli,
21Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo
22Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja,
23Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse
24Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti,
25Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu
26Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu,
27Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu,
28Adani alowa mu Ayati
29Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti,
30Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu!
31Anthu a ku Madimena akuthawa;
32Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu;
33Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse,
34Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira;