1Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola
2Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino
3Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala,
4Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu.
5Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli.
6Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa,
7Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa,
8Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa;
9ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri.
10Wokondedwayo ine ndine wake,
11Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi,
12Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa,
13Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino,