1Pulumutseni Inu Mulungu,
2Ine ndikumira mʼthope lozama
3Ndafowoka ndikupempha chithandizo;
4Iwo amene amadana nane popanda chifukwa
5Mukudziwa uchitsiru wanga, Inu Mulungu,
6Iwo amene amadalira Inu
7Pakuti ndimapirira kunyozedwa chifukwa cha Inu,
8Ndine mlendo kwa abale anga,
9pakuti changu chochitira nyumba yanu chandiphetsa
10Pamene ndikulira ndi kusala kudya,
11pomwe ndavala chiguduli,
12Iwo amene amakhala pa chipata amandinena,
13Koma ndikupempha kwa Inu Ambuye,
14Mundilanditse kuchoka mʼmatope,
15Musalole kuti chigumula chindimeze,
16Ndiyankheni Inu Yehova mwa ubwino wanu wa chikondi chanu;
17Musabisire nkhope yanu mtumiki wanu,
18Bwerani pafupi ndi kundilanditsa;
19Inu mukudziwa momwe ndanyozedwera,
20Mnyozo waswa mtima wanga
21Iwo anayika ndulu mʼchakudya changa
22Chakudya chomwe chayikidwa patsogolo pawo chikhale msampha;
23Maso awo adetsedwe kotero kuti asaonenso
24Khuthulirani ukali wanu pa iwo;
25Malo awo akhale wopanda anthu
26Pakuti iwo amazunza amene inu munamuvulaza
27Awonjezereni kulakwa pa kulakwa kwawo,
28Iwo afufutidwe mʼbuku la amoyo
29Ndikumva zowawa ndi kuzunzika;
30Ine ndidzatamanda dzina la Mulungu mʼnyimbo,
31Izi zidzakondweretsa Yehova kupambana ngʼombe,
32Wosauka adzaona ndipo adzasangalala,
33Yehova amamvera anthu osowa
34Kumwamba ndi dziko lapansi zitamanda Iye,
35pakuti Mulungu adzapulumutsa Ziyoni
36ana atumiki ake adzalitenga kukhala cholowa chawo,