1Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira;
2Apereka cholowa chathu kwa obwera,
3Takhala amasiye ndi wopanda abambo,
4Tiyenera kugula madzi amene timamwa,
5Otilondola atigwira pakhosi;
6Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya
7Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale,
8Akapolo akutilamulira,
9Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe
10Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo,
11Amayi agwiriridwa mu Ziyoni,
12Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo,
13Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu;
14Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda;
15Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu;
16Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu.
17Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi,
18pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja,
19Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya;
20Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse?
21Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere;
22pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu,